Langwan Piksy Tsoka Liyenda Lyrics


Tsoka Liyenda by Langwan Piksy

Kumbire adanka nawo
Palibe akanakhonza
Anasiya pa dzuwa anawo
Anayesa ndi malodza
Ankati satana
Wakhala pa nsana
Kuyamba kudana
Kufuna kuphana
Kuthana
Nzosauzana
Nthawi yakwana
Buluzi wa easy chitseko cha mpana

CHORUS
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Ayo
Tsoka Liyenda
Ayo
Tsoka Liyenda

Bambo awa anali chikhwaya
Ana moyo wawo sanamve kuwawa
Ku school akapita amathawa
Zinavuta ndi za nchere analawa
Yes
Sanauzidwe za moyo
Anapeza bwanji makolo
Chuma
Moyo unakoma
Opanda zo khoma
Kupeza izo afuna
Ohh dzi ana ulesi
Bambo awo atsamira nkono

Akuti zonsezi
Ndi curse
Chayabwa chitedze
Mavuto pang'ono see they stressed
CHORUS
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Ayo
Tsoka Liyenda
Ayo
Tsoka Liyenda

Mudziwaphunzitsa ana
SKupangira pa mawa
Asamayese ngati ophweka moyo
Mukadzapita adzakhala akapolo

Musama yiwale
Kuti zanu munapanga kale
Nzeru zanu sizingatsale
Mungadzavutitse abale
Mdzakolola zomwe mudzale
Chuma ichi sangasamale
Ngati panopa simuphunzitsa
Mapangidwe ake mukumpusitsa
Tsoka ilo
CHORUS
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Anapita ndi nyanga zomwe kumanda
Ayo
Tsoka Liyenda
Ayo
Tsoka Liyenda

Recently Searched Lyrics

Recently Viewed Lyrics